Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 1:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo asende nsembe yopsereza, ndi kuikadzula ziwalo zace.

7. Ndipo ana a Aroni asonkhe mota pa guwa la nsembe, ndi kukonza nkhuni pamotopo;

8. ndi ana a Aroni, ansembewo, akonze ziwalozo, mutu, ndi mafuta pa nkhuni ziri pa mota wa pa guwa la nsembe;

9. koma atsuke ndi madzi matumbo ace ndi miyendo yace; ndi wansembe atenthe zonsezi pa guwa la nsembe, zikhale nsembe yopsereza, nsembe yamoto, ya pfungo lokoma la kwa Yehova.

10. Ndipo copereka cace cikakhala ca nkhosa, kapena ca mbuzi, cikhale nsembe yopsereza; azibwera nayo yaimuna yopanda cirema.

11. Ndipo aiphere iyo pa mbali ya kumpoto ya guwa la nsembe, pamaso pa Yehova; ndipo ana a Aroni, ansembewo, awaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 1