Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 8:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Mwana wa ng'ombe wako wakutaya, Samariya iwe; mkwiyo wanga wayakira iwo; adzalephera kuyera mtima mpaka liti?

6. Pakuti ici comwe cafumira kwa Israyeli; mmisiri wampanga, koma sali Mulungu; inde mwana wa ng'ombe wa Samariya adzaphwanyika-phwanyika.

7. Pakuti abzala mphepo, nadzakolola kabvumvulu; alibe tirigu wosasenga; ngala siidzaturutsa ufa; cinkana iuturutsa, alendo adzaumeza.

8. Israyeli wamezedwa; tsopano ali mwa amitundu ngati cotengera coti munthu sakondwera naco.

9. Pakuti anakwera kumka ku Asuri, ngati mbidzi ya pa yokha mwini wace; Efraimu walembera omkonda ngati anchito.

10. Inde angakhale alembera mwa amitundu ndidzawasonkhanitsa tsopano; ndipo ayamba kucepa cifukwa ca katundu wa mfumu ya akalonga.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 8