1. Lipenga kukamwa kwako, Akudza ngati ciombankhanga, kulim bana ndi nyumba ya Yehova; cifukwa analakwira cipangano canga, napikisana naco cilamulo canga.
2. Adzapfuulira kwa Ine, Mulungu wanga, ife Aisrayeli tikudziwani.
3. Israyeli wacitaya cokoma, mdani adzamlondola.
4. Analonga mafumu, koma sikunacokera kwa Ine; anaika akalonga, koma sindinadziwa; anadzipangira mafano a siliva wao ndi golidi wao, kuti akalikhidwe.