Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 8:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Lipenga kukamwa kwako, Akudza ngati ciombankhanga, kulim bana ndi nyumba ya Yehova; cifukwa analakwira cipangano canga, napikisana naco cilamulo canga.

2. Adzapfuulira kwa Ine, Mulungu wanga, ife Aisrayeli tikudziwani.

3. Israyeli wacitaya cokoma, mdani adzamlondola.

4. Analonga mafumu, koma sikunacokera kwa Ine; anaika akalonga, koma sindinadziwa; anadzipangira mafano a siliva wao ndi golidi wao, kuti akalikhidwe.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 8