Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 4:2-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Koma kulumbira, ndi kunama, ndi kupha, ndi kuba, ndi kucita cigololo; aboola, ndi mwazi ukhudzana nao mwazi.

3. Cifukwa cace dziko lidzacita cisoni, ndi ali yense wokhalamo adzalefuka, pamodzi ndi nyama za kuthengo, ndi mbalame za m'mlengalenga; ndi nsomba za m'nyanja zomwe zidzacotsedwa.

4. Koma munthu asatsutsane ndi mnzace, kapena kudzudzula mnzace; popeza anthu ako ndiwo akunga otsutsana ndi wansembe.

5. Ndipo udzakhumudwa usana, ndi mneneri yemwe adzakhumudwa pamodzi ndi iwe usiku; ndipo ndidzaononga mai wako.

6. Anthu anga aonongeka cifukwa ca kusadziwa; popeza unakana kudziwa, Inenso ndikukaniza, kuti usakhale wansembe wanga; popeza waiwala cilamulo ca Mulungu wako, Inenso ndidzaiwala ana ako.

7. Monga anacuruka, momwemo anandicimwira; ndidzasanduliza ulemerero wao ukhale manyazi.

8. Adyerera cimo la anthu anga, nakhumbira cosalungama cao, yense ndi mtima wace.

9. Ndipo kudzakhala monga anthu, momwemo wansembe; ndipo ndidzawalanga cifukwa canjira zao, ndi kuwabwezera macitidwe ao.

10. Ndipo adzadya, koma osakhuta; adzacita cigololo, koma osacuruka; pakuti waleka kusamalira Yehova.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 4