Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 2:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Nenani kwa abale anu, Anthu anga, ndi kwa alongo anu, Wocitidwa-cifundo.

2. Mutsutsane naye mai wanu, mutsutsane naye; pakuti sali mkazi wanga, ndi Ine sindiri mwamuna wace; ndipo acotse zadama zace pankhope pace, ndi zigololo zace pakati pa maere ace;

3. ndingambvule wamarisece, ndi kumuika ngati tsiku lija anabadwalo, ndi kumsanduliza ngati cipululu, ndi kumuika ngati dziko louma, ndi kumupha nalo ludzu;

4. ndipo ana ace sindidzawacitira cifundo; pakuti iwo ndiwo ana acigololo.

5. Pakuti mai wao anacita cigololo; iye amene anali ndi pakati pa iwo anacita camanyazi; pakuti anati, Ndidzatsata ondikondawo, akundipatsa ine cakudya canga, ndi madzi anga, ubweya wanga, ndi thonje langa, mafuta anga, ndi cakumwa canga.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 2