3. Asuri sadzatipulumutsa; sitidzayenda pa akavalo, ndipo sitil dzanenanso kwa nchito ya manja athu, Inu ndinu milungu yathu; pakuti mwa Inu ana amasiye apeza cifundo.
4. Ndidzaciritsa kubwerera kwao, ndidzawakonda mwaufulu; pakuti mkwiyo wanga wamcokera.
5. Ndidzakhala kwa Israyeli ngati mame; adzacita maluwa ngati kakombo, ndi kutambalalitsa mizu yace ngati Lebano.
6. Nthambi zace zidzatambalala, ndi kukoma kwace kudzanga kwa mtengo waazitona, ndi pfungo lace ngati Lebano.