Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 14:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Mukani nao mau, nimubwerere kwa Yehova; nenani kwa Iye, Cotsani mphulupulu zonse, nimulandire cokoma; ndipo tidzapereka mau milomo yathu ngati: ng'ombe.

3. Asuri sadzatipulumutsa; sitidzayenda pa akavalo, ndipo sitil dzanenanso kwa nchito ya manja athu, Inu ndinu milungu yathu; pakuti mwa Inu ana amasiye apeza cifundo.

4. Ndidzaciritsa kubwerera kwao, ndidzawakonda mwaufulu; pakuti mkwiyo wanga wamcokera.

5. Ndidzakhala kwa Israyeli ngati mame; adzacita maluwa ngati kakombo, ndi kutambalalitsa mizu yace ngati Lebano.

6. Nthambi zace zidzatambalala, ndi kukoma kwace kudzanga kwa mtengo waazitona, ndi pfungo lace ngati Lebano.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 14