Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 1:9-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo Yehova anati, Umuche dzina lace Si-anthuanga; pakuti inu sindinu anthu anga, ndipo Ine sindine wanu.

10. Angakhale anatero, kuwerenga kwace kwa ana a Israyeli kudzanga mcenga wa kunyanja, wosayeseka kapena kuwerengeka; ndipo kudzatero kuti m'mene adawanena, Simuli anthu anga, adzanena nao, Muli ana a Mulungu wamoyo.

11. Ndipo ana a Yuda ndi ana a Israyeli adzasonkhanidwa pamodzi, nadzadziikira mkuru mmodzi, nadzakwera kucoka m'dziko; pakuti tsiku la Yezreeli ndi lalikuru.

Werengani mutu wathunthu Hoseya 1