Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Habakuku 2:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Udzazidwa nao manyazi m'malo mwa ulemerero; imwa iwenso, nukhale wosadulidwa; cikho ca dzanja lamanja la Yehova cidzatembenukira iwe, ndi kusanza kwa manyazi kudzakhala pa ulemerero wako,

17. Pakuti ciwawa cidacitikira Lebano cidzakukuta, ndi cionongeko ca nyama cidzakuopsa; cifukwa ca mwazi wa anthu, ndi ciwawa cocitidwira dziko, mudzi, ndi onseokhalamo.

18. Apindulanji nalo fano losema, kuti wakulipanga analisema; fano loyenga ndi mphunzitsi wamabodza, kuti wakulipanga alikhulupirira, ata panga matafano osanena mau?

19. Tsoka iye wakunena kwa mtengo, Galamuka; ndi kwa mwala wosalankhula, Nyamuka Kodi ici ciphunzitsa? Taona cakutidwa ndi golidi ndi siliva, ndi m'kati mwace mulibe mpweya konse.

Werengani mutu wathunthu Habakuku 2