Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Habakuku 2:11-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pakuti mwala wa m'khoma upfuula, ndi mtanda wa kuphaso udzaubvomereza.

12. Tsoka tye wakumanga mudzindi mwazi, nakhazikitsa mudzi ndi cisalungamo!

13. Taonani, sicicokera kwa Yehova wa makamu kodi kuti mitundu ya anthu ingogwirira moto nchito, ndi anthu angodzilemetsa pa zopanda pace?

14. Pakuti dziko lapansi lidzadzazidwa ndi cidziwitso ca ulemerero wa Yehova, monga madzi aphimba pansi panyanja.

15. Tsoka wakuninkha mnzace cakumwa, ndi kuonjezako mankhwala ako, ndi kumledzeretsa, kuti upenyerere manyazi ao!

16. Udzazidwa nao manyazi m'malo mwa ulemerero; imwa iwenso, nukhale wosadulidwa; cikho ca dzanja lamanja la Yehova cidzatembenukira iwe, ndi kusanza kwa manyazi kudzakhala pa ulemerero wako,

17. Pakuti ciwawa cidacitikira Lebano cidzakukuta, ndi cionongeko ca nyama cidzakuopsa; cifukwa ca mwazi wa anthu, ndi ciwawa cocitidwira dziko, mudzi, ndi onseokhalamo.

18. Apindulanji nalo fano losema, kuti wakulipanga analisema; fano loyenga ndi mphunzitsi wamabodza, kuti wakulipanga alikhulupirira, ata panga matafano osanena mau?

19. Tsoka iye wakunena kwa mtengo, Galamuka; ndi kwa mwala wosalankhula, Nyamuka Kodi ici ciphunzitsa? Taona cakutidwa ndi golidi ndi siliva, ndi m'kati mwace mulibe mpweya konse.

Werengani mutu wathunthu Habakuku 2