23. Semu ndi Yafeti ndipo anatenga copfunda, naciika pa mapewa ao a onse awiri, nayenda cambuyo, napfunditsa umarisece wa atate wao: nkhope zao zinali cambuyo, osaona umarisece wa atate ao.
24. Nowa ndipo anauka kwa kuledzera kwace, nadziwa cimene anamcitira iye mwana wace wamng'ono.
25. Ndipo anati,Wotembereredwa ndi Kanani:Adzakhala kwa abale ace kapolo wa akapolo:
26. Ndipo anati:Ayamikike Yehova, Mulungu wa Semu;Kanani akhale kapolo wace.
27. Mulungu akuze Yafeti,Akhale iye m'mahema a Semu; Kanani akhale kapolo wace.
28. Ndipo Nowa anakhala ndi moyo cigumula citapita, zaka mazana atatu kudza makumi asanu.
29. Ndipo masiku onse a Nowa anali mazana asanu ndi anai kudza makumi asanu: ndipo anamwalira.