Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 9:23-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Semu ndi Yafeti ndipo anatenga copfunda, naciika pa mapewa ao a onse awiri, nayenda cambuyo, napfunditsa umarisece wa atate wao: nkhope zao zinali cambuyo, osaona umarisece wa atate ao.

24. Nowa ndipo anauka kwa kuledzera kwace, nadziwa cimene anamcitira iye mwana wace wamng'ono.

25. Ndipo anati,Wotembereredwa ndi Kanani:Adzakhala kwa abale ace kapolo wa akapolo:

26. Ndipo anati:Ayamikike Yehova, Mulungu wa Semu;Kanani akhale kapolo wace.

27. Mulungu akuze Yafeti,Akhale iye m'mahema a Semu; Kanani akhale kapolo wace.

28. Ndipo Nowa anakhala ndi moyo cigumula citapita, zaka mazana atatu kudza makumi asanu.

29. Ndipo masiku onse a Nowa anali mazana asanu ndi anai kudza makumi asanu: ndipo anamwalira.

Werengani mutu wathunthu Genesis 9