Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 9:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, Ici ndici cizindikiro ca pangano ndalikhazikitsa popaogana ndi Ine ndi zamoyo zonse za pa dziko lapansi.

18. Ndi ana amuna a Nowa amene anaturuka m'cingalawa ndiwo Semu, ndi Hamu, ndi Yafeti: Hamu ndiye atate wace wa Kanani.

19. Amenewa ndiwo ana amuna atatu a Nowa: ndiwo anafalikira dziko lonse lapansi.

20. Ndipo anayamba Nowa kukhala munthu wakulima nthaka, ndipo analima munda wamphesa:

21. namwa vinyo wace, naledzera; ndipo anali wamarisece m'kati mwa bema wace.

22. Ndipo Hamu atate wace wa Kanani, anauona umarisece wa atate wace, nauza abale ace awiri amene anali kunja.

Werengani mutu wathunthu Genesis 9