Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 8:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. ndipo madzi anaphweraphwerabe pa dziko lapansi: pamene anatha masiku zana limodzi kudza makumi atatu madzi anacepa.

4. Ndipo cingalawa cinaima pa mapiri a Ararati, mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku lakhumi ndi asanu ndi awiri la mwezi.

5. Ndipo madzi analinkucepa kufikira mwezi wakhumi; mwezi wakhumi tsiku loyamba mwezi ndipo padaoneka mitu ya mapiri.

6. Ndipo panali atapita masiku makumi anai, Nowa anatsegula pa zenera la cingalawa limene analipanga:

7. ndipo anaturutsa khungubwe, ndipo anaturuka kunka kwina ndi kwina kufikira adaphwa madzi pa dziko lapansi,

8. Ndipo anaturutsa njiwa imcokere, kuti aone kapena madzi anaphwa pamwamba pa dziko lapansi;

Werengani mutu wathunthu Genesis 8