Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 8:20-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo Nowa anamanga guwa la nsembe la Yehova; natengapo nyama zodyedwa zonse ndi mbalame zodyedwa zonse napereka nsembe zopsereza paguwapo.

21. Ndipo Yehova anamva conunkhira cakukondweretsa; nati Yehova m'mtima mwace, Sindidzatembereranso konse nthaka cifukwa ca munthu; pakuti ndingaliro ya mtima wa munthu iri yoipa kuyambira pa unyamata wace; sindidzaphanso konse zinthu zonse zamoyo, monga momwe ndacitiramo.

22. Pakukhalabe masiku a dziko lapansi, nthawi yakubzala ndi yakukunkha, cisanu ndi mafundi, malimwe ndi msakasa, usana ndi usiku sizidzalekai.

Werengani mutu wathunthu Genesis 8