Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 8:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Turukamoni m'cingalawamo, iwe ndi ana ako, ndi mkazi wako, ndi akazi a ana ako pamodzi ndi iwe.

17. Turutsa pamodzi ndi iwe zamoyo zonse ziti ndi iwe za nyama zonse, zouluka, ndi zinyama, ndi zokwawa zonse zakukwawa pa dziko lapansi; kuti ziswane pa dziko lapansi, zibalane, zicuruke pa dziko lapansi.

18. Ndipo anaturuka Nowa ndi ana ace, ndi mkazi wace, ndi akazi a ana ace, pamodzi naye:

19. zinyama zonse, zokwawa zonse, zouluka zonse, ndi zonse zokwawa pa dziko lapansi, monga mwa mitundu yao, zinaturuka m'cingalawamo.

Werengani mutu wathunthu Genesis 8