Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 6:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Koma Nowa anapeza ufulu pamaso pa Yehova.

9. Mibadwoya Nowandiiyi: Nowa anali munthu wolungama ndi wangwiro m'mibadwo yace; Nowa anayendabe ndi Mulungu.

10. Ndipo Nowa anabala ana amuna atatu, Semu, Hamu ndi Yafeti.

11. Ndipo dziko lapansi linabvunda pamaso pa Mulungu, dziko lapansi ndipo linadzala ndi ciwawa.

12. Ndipo Mulungu anaona dziko lapansi, ndipo taonani, linabvunda; pakuti anthu onse anabvunditsa njira yao pa dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Genesis 6