Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 50:9-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo anakwera pamodzi ndi iye magareta ndi apakavalo; ndipo panali khamc lalikuru.

10. Ndipo anafika pa dwale la Atadi, liri tsidya lija la Yordano, pamenepo anamlira maliro a atate wace masiku asanu ndi limodzi.

11. Ndipo pamene anthu okhala m'dzikomo; Akanani, anaona maliro a m'dwale la Atadi, anati, Awa ndi maliro akuru a Aaigupto: cifukwa cace dzina la pamenepo linachedwa Abeli-mizraimu, pali tsidya lija la Yordano.

12. Ndipo ana ace amuna anamcitira iye monga anawalamulira iwo;

13. cifukwa kuti ana ace amuna anamnyamula iye kulowa naye m'dziko la Kanani, ndi kumuika iye m'phanga la munda wa Makipela, limene Abrahamu analigula pamodzi ndi munda, likhale poikira pace, kwa Efroni Mhiti, patsogolo pa Mamre.

14. Ndipo ataika atate wace, Yosefe mabwera ku Aigupto, iye ndi abale ace, ndi onse amene anakwera pamodzi naye kukaika atate wace.

15. Ndipo pamene abale ace a Yosefe anaona kuti atate wao anafa, anati, Kapena Yosefe adzatida ife, ndipo adzatibwezera ife zoipa zonse tidamcitira iye.

Werengani mutu wathunthu Genesis 50