Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 50:24-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Yosefe ndipo anati kwa abale ace, Ndirinkufa ine, koma Mulungu adzaonekera kwa inu, adzakucotsani inu m'dziko muno kubwera kunka ku dziko limene analumbirira kwa Abrahamu ndi kwa Isake, ndi kwa Yakobo

25. Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israyeli kuti, Mulungu adzaonekera kwa inu ndithu, ndipo mudzakwera nao mafupa anga kucokera kuno.

26. Ndipo anafa Yosefe, anali wa zaka zana limodzi ndi khumi; ndipo anakonza thupi lace ndi mankhwala osungira, ndipo ariamuika iye m'bokosi m'Aigupto.

Werengani mutu wathunthu Genesis 50