Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 50:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yosefe anagwapa nkhope ya atate wace, namlirira iye nampsompsona iye.

2. Ndipo Yosefe anauza akapolo ace asing'anga kutiakonze atate wace: ndi mankhwala osungira thupi: ndipo asing'anga anakonza Israyeli.

3. Ndipo anatha masiku ace makumi anai a iye; cifukwa comweco amatsiriza masiku akukonza thupi; ndipo Aaigupto anamlira iye masiki makumi asanu ndi awiri.

4. Atapita masiku akumlira iye Yosefe anati kwa mbumba ya Farao kuti, Ngatitu ndapeza ufulu pamase panu, nenanitu m'makutu a Parae kuti,

5. Atate wanga anandilumbi ritsa ine, kuti, Taona, ndirinkufa m'manda m'mene ndadzikonzeran ndekha m'dziko la Kanani, m'menemo udzandiika ine. Tsopano mundi loletu, ndikwereko, ndipite, ndikaike atate wanga, nditatero ndidzabwe ranso.

6. Ndipo Farao anati, Pita kaike atate wako, monga iye anaku lumbiritsa iwe.

7. Ndipo Yosefe anapita kukaika atate wace; ndipo anakwera pamodzi ndi akapolo onse a Farao, ndi akuru a pa mbumba yace, ndi akuru onse a m'dziko la Aigupto,

8. ndi mbumba yonse ya Yosefe ndi abale ace, ndi mbumba ya atate wace: ang'ono ao okha, ndi nkhosa zao, ndi ng'ombe zao, anazisiya m'dziko la Goseni.

9. Ndipo anakwera pamodzi ndi iye magareta ndi apakavalo; ndipo panali khamc lalikuru.

Werengani mutu wathunthu Genesis 50