Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 49:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Yuda ndi mwana wa mkango,Kucokera kuzomotola, mwananga, wakwera;Anawerama pansi, anabwatama ngati mkango,Ndipo ngati mkango waukazi; ndani adzamukitsa iye?

10. Ndodo yacifumu siidzacoka mwa Yuda,Kapena wolamulira pakati pa mapazi ace,Kufikira atadza Silo;Ndipo anthu adzamvera iye.

11. Adamanga mwana wa kavalo wace pampesa,Ndi mwana wa buru wace pa mpesa wosankhika;Natsuka malaya ace m'vinyo,Ndi copfunda cace m'mwazi wa mphesa.

12. Maso ace adzafiira ndi vinyo,Ndipo mana ace adzayera ndi mkaka.

13. Zebuloni adzakhala m'doko la kunyanja;Ndipo iye adzakhala doko la ngalawa;Ndipo malire ace adakhala pa Zidoni.

14. Isakara ndiye buru wolimba,Alinkugona pakati pa makola;

Werengani mutu wathunthu Genesis 49