Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 49:8-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Yuda, abale ako adzakuyamika iwe;Dzanja lako lidzakhala pa khosi la adani ako;Ana amuna a atate wako adzakuweramira.

9. Yuda ndi mwana wa mkango,Kucokera kuzomotola, mwananga, wakwera;Anawerama pansi, anabwatama ngati mkango,Ndipo ngati mkango waukazi; ndani adzamukitsa iye?

10. Ndodo yacifumu siidzacoka mwa Yuda,Kapena wolamulira pakati pa mapazi ace,Kufikira atadza Silo;Ndipo anthu adzamvera iye.

11. Adamanga mwana wa kavalo wace pampesa,Ndi mwana wa buru wace pa mpesa wosankhika;Natsuka malaya ace m'vinyo,Ndi copfunda cace m'mwazi wa mphesa.

12. Maso ace adzafiira ndi vinyo,Ndipo mana ace adzayera ndi mkaka.

13. Zebuloni adzakhala m'doko la kunyanja;Ndipo iye adzakhala doko la ngalawa;Ndipo malire ace adakhala pa Zidoni.

14. Isakara ndiye buru wolimba,Alinkugona pakati pa makola;

15. Ndipo anaona popumulapo kuti panali pabwino,Ndi dziko kuti linali lokondweretsa;Ndipo anaweramitsa phewa lace kuti anyamule,Nakhala kapolo wakugwira nchito ya msonkho,

16. Dani adzaweruza anthu ace,Monga limodzi la mafuko a Israyeli.

17. Dani adzakhala njoka m'khwalala,Songo panjira,Imene iluma zitende za kavalo,Kuti womkwera wace agwe cambuyo.

18. Ndadikira cipulumutso canu, Yehova.

19. Ndi Gadi, acifwamba adzampsinja iye;Koma iye adzapsinja pa citende cao.

20. Ndi Aseri, cakudya cace ndico mafuta,Ndipo adzapereka zolongosoka zacifumu.

21. Nafitali ndi nswala yomasuka;Apatsa mau abwino.

22. Yosefe ndi nthambi yobala,Nthambi yobala pambali pa kasupe;Nthambi zace ziyangayanga palinga.

23. Eni uta anabvutitsa iye kwambiri,Namponyera iye, namzunza:

Werengani mutu wathunthu Genesis 49