15. Ndipo anaona popumulapo kuti panali pabwino,Ndi dziko kuti linali lokondweretsa;Ndipo anaweramitsa phewa lace kuti anyamule,Nakhala kapolo wakugwira nchito ya msonkho,
16. Dani adzaweruza anthu ace,Monga limodzi la mafuko a Israyeli.
17. Dani adzakhala njoka m'khwalala,Songo panjira,Imene iluma zitende za kavalo,Kuti womkwera wace agwe cambuyo.
18. Ndadikira cipulumutso canu, Yehova.
19. Ndi Gadi, acifwamba adzampsinja iye;Koma iye adzapsinja pa citende cao.
20. Ndi Aseri, cakudya cace ndico mafuta,Ndipo adzapereka zolongosoka zacifumu.
21. Nafitali ndi nswala yomasuka;Apatsa mau abwino.
22. Yosefe ndi nthambi yobala,Nthambi yobala pambali pa kasupe;Nthambi zace ziyangayanga palinga.
23. Eni uta anabvutitsa iye kwambiri,Namponyera iye, namzunza:
24. Koma uta wace unakhala wamphamvu,Ndi mikono ya manja ace inalimbitsidwaNdi manja a Wamphamvu wa Yakobo.(Kucokera kumeneko ndi mbusa, mwala wa Israyeli,)
25. Ndi Mulungu wa atate wako amene adzakuthangata iwe,Ndi Wamphamvuyonse, amene adzakudalitsa iweNdi madalitso a Kumwamba,Madalitso a madzi akuya akukhala pansi,Madalitso a mabere, ndi a mimba.
26. Madalitso a atate wakoApambana mphamvu ndi madalitso a makolo anga,Kufikira ku malekezero a patari a mapiri a cikhalire;Adzakhala pa mutu wa Yosefe,Ndi pakati pa mutu wa iye amene ali wolekanitsidwa ndi abale ace.
27. Benjamini ndiye mmbulu wakulusalusa;M'mamawa adzadya comotola,Madzulo adzagawa zofunkha.
28. Awa onse ndiwo mafuko khumi ndi awiri a Israyeli: izo ndizo zomwe ananena kwa iwo atate wao nawadalitsa; yense monga mdalitso wace anawadalitsa.
29. Ndipo analangiza iwo nati kwa iwo, Ine nditi ndisonkhanizidwe kwa anthu a mtundu wanga; mundiike ine pamodzi ndi makolo anga m'phanga liri m'munda wa Efroni Mhiti,