Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 46:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo Yakobo anacoka ku Beereseba, ndipo ana amuna a Israyeli anamnyamula Yakobo atate wao, ndi ana ao ang'ono, ndi akazi ao, m'magareta amene Farao anatumiza kuti amnyamule iye,

6. Ndipo anatenga ng'ombe zao ndi cuma cao anacipezam'dziko la Kanani, nadza ku Aigupto, Yakobo ndi mbeu zace zonse pamodzi ndi iye;

7. ana ace amuna, ndi zidzukulu zace zazimuna, ndi ana akazi ace, ndi zidzukulu zace zazikazi, ndi mbeu zace zonse anadza nazo m'Aigupto.

8. Maina a ana a Israyeli amene anadza m'Aigupto ndi awa: Yakobo ndi ana amuna ace: Rubeni mwana wamwamuna woyamba wa Yakobo.

9. Ndi ana amuna a Ruberu Hanoki, ndi Palu, ndi Hezroni, ndi Karmi.

10. Ndi ana amuna a Simeoni: Yemueli ndi Yamini, ndi Ohadi, ndi Yakini, ndi Zohari, ndi Sauli, mwana wamwamuna wa mkazi wa ku Kanani.

11. Ndi ana amuna a Levi: Gerisoni, Kohati, ndi Merai.

Werengani mutu wathunthu Genesis 46