Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 46:31-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Ndipo Yosefe anati kwa abale ace, ndi kwa mbumba ya atate wace, Ndidzanka, ndikauze Farao, ndipo ndidzati kwa iye, Abale anga ndi mbumba ya atate wanga, amene anali m'dziko la Kanani, afika kwa ine;

32. ndipo anthuwo ali abusa cifukwa anakhala oweta ng'ombe; ndipo anadza ndi nkhosa zao ndi ng'ombe zao ndi zonse ali nazo.

33. Ndipo padzakhala pamene Farao adzaitana inu, nadzati, Nchito yanu njotani?

34. mudzati, Akapolo anu akhala oweta ng'ombe ciyambire ubwana wathu kufikira tsopano, ife ndi atate athu; kuti mukhale m'dziko la Goseni; a cifukwa abusa onse anyansira Aaigupto.

Werengani mutu wathunthu Genesis 46