Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 46:11-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndi ana amuna a Levi: Gerisoni, Kohati, ndi Merai.

12. Ndi ana amuna a Yuda: Eri, ndi Onani, ndi Sela, ndi Perezi, ndi Zera; koma Eri ndi Onani anafa m'dziko la Kanani. Ndi ana amuna a Perezi ndiwo Hezroni ndi Hamuli.

13. Ndi ana amuna a Isakara: Tola ndi Puva, ndi Yabi, ndi Simroni.

14. Ndi ana amuna a Zebuloni: Seredi, ndi Eloni ndi Yaledi.

15. Amenewo ndi ana amuna a Leya, amene anambalira Yakobo m'Padanaramu, pamodzi ndi mwana wamkazi wace Dina; ana amuna ndi akazi onse: ndiwo anthu makumi atatu kudza atatu.

16. Ndi ana amuna a Gadi: Zifioni, ndi Hagi, ndi Suni, ndi Ezboni, ndi Eri, ndi Arodi, ndi Areli.

17. Ndi ana amuna a Aseri: Yimna, ndi Yisiva, ndi Yisivi, ndi Beriya, ndi Sera mlongo wao; ndi ana a Beriya: Hebere, ndi Maliki eli.

18. Amenewa ndi ana a Zilipa, amene Labani anampatsa Leya mwana wace wamkazi, amenewo anambalira Yakobo, anthu khumi ndi asanu ndi mmodzi.

19. Ana a Rakele mkazi wace wa Yakobo: Yosefe ndi Benjamini.

20. Kwa Yosefe kunabadwa m'dziko la Aigupto Manase ndi Efraimu, amene Asenati mwana wamkazi wa Potifera wansembe wa Oni anambalira iye.

21. Ndi ana amuna a Benjamini: Bela ndi Bekeri, ndi Asibeli, ndi Gera, ndi Namani, ndi Ehi ndi Rosi, Mupimu ndi Hupimu, ndi Aridi.

22. Amenewo ndi ana a Rakele, amene anabadwira Yakobo; anthu onse ndiwo khumi ndi anai.

23. Ndi ana amuna a Dani: Husimu.

24. Ndi ana amuna a Nafitali: Yazeeli, ndi Guni, ndi Yezera ndi Silemu.

25. Amenewa ndi ana a Biliha, amene Labani anampatsa Rakele mwana wace wamkazi, amenewo anambalira Yakobo; anthu onse ndiwo asanu ndi awiri.

Werengani mutu wathunthu Genesis 46