Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 45:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo ana a Israyeli anacita cotero: ndipo Yosefe anawapatsa iwo magareta monga analamulira Farao, nawapatsa phoso la panjira,

22. Onse anawapatsa yense zobvala zopindula; koma Benjamini anampatsa ndalama zasiliva mazana atatu ndi zobvala zopindula zisanu.

23. Kwa atate wace anatumiza zotere: aburu khumi osenza zinthu zabwino za m'Aigupto, ndi aburu akazi khumi osenza tirigu, ndi cakudya, ndi phoso la atate la panjira.

24. Ndipo anamukitsa abale ace, ndipo anacoka; ndipo anati kwa iwo, Musakangane panjira.

Werengani mutu wathunthu Genesis 45