19. Tsopano mwalamulidwa citani ici; muwatengere ana anu ndi akazi magareta a m'dziko la Aigupto; nimubwere naye atate wanu.
20. Musasamalire cuma canu; popeza zabwino za dziko lonse la Aigupto ndi zanu.
21. Ndipo ana a Israyeli anacita cotero: ndipo Yosefe anawapatsa iwo magareta monga analamulira Farao, nawapatsa phoso la panjira,
22. Onse anawapatsa yense zobvala zopindula; koma Benjamini anampatsa ndalama zasiliva mazana atatu ndi zobvala zopindula zisanu.
23. Kwa atate wace anatumiza zotere: aburu khumi osenza zinthu zabwino za m'Aigupto, ndi aburu akazi khumi osenza tirigu, ndi cakudya, ndi phoso la atate la panjira.