Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 44:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Nuike cikho canga, cikho casiliva ciija, kukamwa kwa thumba la wamng'ono, pamodzi ndi ndalama za tirigu zace. Ndipo iye anacita monga mau ananena Yosefe.

3. Pamene kudaca, anamukitsa anthu iwo ndi aburu ao.

4. Ataturuka m'mudzi asanamuke patari, Yosefe anati kwa tsanyumba wace, Tanyamuka, talondola anthu aja, ukawapeza unene nao, Cifukwa canji mwabwezera zoipa m'malo mwa zabwino?

5. Kodi si ndico comwera naco mbuyanga, naombeza ula naco? Mwacitira coipa pakutero.

6. Ndipo anapeza iwo, nanena nao mau omwewo.

7. Nati kwa iye, Bwanji mbuyanga anena mau otere? Ngati nkutheka kuti akapolo anu acite cotero?

Werengani mutu wathunthu Genesis 44