Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 43:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. mutengenso mphwanu, nimuoyamuke, mupitenso kwa munthu uja:

14. Mulungu Wamphamvuyonse adzakupatsani inu cifundo pamaso pa munthu uja, kuti akumasulireni inu mbale wanu wina ndi Benjamini. Ndipo ine, ngati ndikhala wopanda ana, ndikhalatu.

15. Amunawo ndipo anatenga mphatso, natenga ndalama zowirikiza m'manja mwao, ndi Benjamini; ndipo ananyamuka ndi kutsikira ku Aigupto, naima pamaso pa Yosefe.

16. Ndipo pamene anaona Benjamini pamodzi nao, anati kwa tsanyumba wace, Lowa nao anthuwo m'nyumba, kaphere iwo, kakoozere, cifukwa anthuwo adzadya ndi ine usana uno.

Werengani mutu wathunthu Genesis 43