Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 42:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Yosefe anali wolamulira dziko; ndiye amene anagulitsa kwa anthu onse a m'dziko; ndipo anafika abale ace a Yosefe, namweramira pansi, nkhope zao pansi.

7. Ndipo Yosefe anaona abale ace, ndipo anazindikira iwo, koma anadziyesetsa kwa iwo ngati mlendo, nanena kwa iwo mwankhanza: ndipo anati kwa iwo, Mufuma kuti inu? nati iwo, Ku dziko la Kanani kudzagula cakudya.

8. Ndipo Yosefe anazindikira abale ace, koma iwo sanamzindikira iye.

9. Ndipo Yosefe anakumbukira maloto amene analoto za iwo, ndipo anati kwa iwo, Ozonda inu; mwadzera kudzaona usiwa wa dziko.

10. Ndipo iwo anati kwa iye, Iai, mbuyanga, koma akapolo anu adzera kudzagula cakudya.

Werengani mutu wathunthu Genesis 42