Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 42:31-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Koma ife tinati kwa iye, Tiru anthu oona; sitiri ozonda;

32. tiri abale khumi ndi awiri, ana a atate wathu; wina palibe, ndipo lero wamng'ono ali ndi atate wathu m'dziko la Kanani.

33. Ndipo munthuyo mwini dziko anati kwa ife, Momwemu ndidzadziwa kuti muli anthu oona; siyani mmodzi wa abale anu pamodzi ndi ine, tengani tirigu wa njala ya kwanu, mukani;

34. idzani naye mphwanu kwa ine, ndipo ndidzadziwa kuti simuli ozonda koma anthu oona: comweco ndidzakubwezerani inu mbale wanu, ndipo mudzacita malonda m'dziko muno.

Werengani mutu wathunthu Genesis 42