Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 42:15-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Mudzayesedwa ndi ici, pali moyo wa Farao, simudzaturuka muno, koma akadze kuno mphwanu ndiko.

16. Tumizani mmodzi wa inu akatenge, adze naye mphwanu: ndipo inu mudzamangidwa kuti mau anu ayesedwe, ngati zoona ziri mwa inu: penatu, pali moyo wa Farao, muli ozonda ndithu.

17. Ndipo anaika onse m'kaidi masiku atatu.

18. Ndipo Yosefe anati kwa iwo tsiku lacitatu, Citani ici, kuti mukhale ndi moyo; ine ndiopa Mulungu;

19. ngati muli oona, mmodzi wa abale anu amangidwe m'kaidi momwemo; mukani inu, mupite naye tirigu wa njala ya mabanja anu;

20. koma mukatenge mphwanu kudza naye kwa ine, kuti atsimikizidwe mau anu ndipo simudzafa. Ndipo anacita comweco.

21. Ndipo iwo anati wina ndi mnzace, Tacimwiratu mbale wathu, pamene tinaona kubvutidwa kwa mtima wace, potipembedzera ife, koma ife tinakana kumvera, cifukwa cace kubvutidwa kumene kwatifikira.

22. Ndipo Rubeni anayankha nati kwa iwo, Kodi sindinanena kwa inu kuti, Musacimwire mwanayu; ndipo inu munakana kumvera? cifukwa cacenso, taonani mwazi wace ufunidwa.

23. Ndipo sanadziwa kuti, Yosefe anamva; cifukwa anali ndi womasulira.

24. Ndipo anawafotokozera iwo nalira, nawatembenukiranso, nanena nao, nampatula Simeoni mwa iwo, nammanga iye pamaso pao.

25. Ndipo Yosefe analamulira kuti adzaze zotengera zao ndi tirigu, ndi kubweza ndalama zao, ali yense m'thumba mwace, ndi kuwapatsa phoso la panjira; ndipo anatero nao.

26. Ndipo anasenzetsa aburu ao tirigu wao nacokapo.

27. Ndipo pamene wina wa iwo anamasula thumba lace kuti adyetse buru wace pacigono, anapeza ndalama zace; taonani, zinali kukamwa kwa thumba lace.

28. Ndipo iye anati kwa abale ace, Wandibwezera ine ndalama zanga, taonani, ziri kukamwa kwa thumba langa; ndipo mitima yao inawadera iwo, nanthunthumira, natembenukirana wina ndi mnzace kuti, Nciani ici Mulungu waticitira ife?

29. Ndipo anadza kwa Yakobo atate wao ku dziko la Kanani, namfotokozera iye zonse zinaonekera kwa iwo;

30. kuti, Munthu mwini dziko, ananena ndi ife mwankharwe, natiyesa ife ozonda dziko.

31. Koma ife tinati kwa iye, Tiru anthu oona; sitiri ozonda;

Werengani mutu wathunthu Genesis 42