Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 42:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anaona Yakobo kuti m'Aigupto munali tirigu, nati Yakobo kwa ana ace amuna, Cifukwa canji mulinkuyang'anana?

2. Ndipo iye anati, Taonani, ndamva kuti m'Aigupto muli tirigu, mutsikireko mutigulire kumeneko; kuti tikhale ndi moyo, tisafe.

3. Ndipo abale ace a Yosefe khumi anatsikira kukagula tirigu m'Aigupto.

4. Koma Yakobo sanamtuma Benjamini mphwace wa Yosefe, pamodzi ndi abale ace, cifukwa anati, Coipa cingamgwere iye.

5. Ndipo ana amuna a Israyeli anadza kudzagula mwa iwo amene anadzako, pakuti m'dziko la Kanani munali njala.

6. Ndipo Yosefe anali wolamulira dziko; ndiye amene anagulitsa kwa anthu onse a m'dziko; ndipo anafika abale ace a Yosefe, namweramira pansi, nkhope zao pansi.

7. Ndipo Yosefe anaona abale ace, ndipo anazindikira iwo, koma anadziyesetsa kwa iwo ngati mlendo, nanena kwa iwo mwankhanza: ndipo anati kwa iwo, Mufuma kuti inu? nati iwo, Ku dziko la Kanani kudzagula cakudya.

8. Ndipo Yosefe anazindikira abale ace, koma iwo sanamzindikira iye.

Werengani mutu wathunthu Genesis 42