28. Ici ndi cinthu cimene ndinena kwa Farao: cimene Mulungu ati acite wasonyeza kwa Farao.
29. Taonani, zidzafika zaka zisanu ndi ziwiri zakucuruka cakudya m'dziko lonse la Aigupto;
30. ndipo pambuyo pao zidzauka zaka zisanu ndi ziwiri za njala; ndipo anthu adzaiwala zocuruka zonsezo m'dziko la Aigupto; ndipo njala idzapululutsa dziko;
31. ndipo zocuruka sizidzazindikirika cifukwa ca njala ikudza m'mbuyoyo, pakuti idzabvuta.
32. Ndipo lotolo linabwezedwa kawiri kwa Farao, cifukwa cinthu ciri cokhazikika ndi Mulungu, ndipo Mulungu afulumira kucicita.