Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 41:24-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. ndipo ngala zoonda zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zabwino; ndipo ndinafotokozera amatsenga: koma panalibe wondimasulira ine.

25. Ndipo Yosefe anati kwa Farao, Loto la Farao liri limodzi: cimene Mulungu ati acite wammasulira Farao.

26. Ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zabwino ndizo zaka zisanu ndi ziwiri, ndi ngala zisanu ndi ziwiri zabwino ndizo zaka zisanu ndi ziwiri: loto liri limodzi.

27. Ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zoonda ndi za maonekedwe oipa zinaturuka pambuyo pao ndizo zaka zisanu ndi ziwiri, ndiponso ngala zisanu ndi ziwiri zopanda kanthu zopsyerera ndi mphepo ya kum'mawa, ndizo zaka zisanu ndi ziwiri za njala.

Werengani mutu wathunthu Genesis 41