Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 40:17-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. m'licelo lapamwamba munali mikate ya Farao ya mitundu mitundu; ndipo mbalame zinadya ya m'licelo la pamutu panga.

18. Ndipo Yosefe anayankha nati, Mmasuliro wace ndi uwu: malicelo atatu ndiwo masiku atatu;

19. akali masiku atatu Farao adzakweza mutu wako ndi kuucotsa, nadzakupacika iwe pamtengo: ndipo mbalame zidzadya mnofu wako.

20. Ndipo panali tsiku lacitatu ndilo tsiku lakubadwa kwace kwa Farao, iye anakonzera anyamata ace madyerero, ndipo anakweza mutu wa wopereka cikho wamkuru, ndi mutu wa wophika mkate wamkuru pakati pa anyamata ace.

21. Ndipo anabwezanso wopereka cikho ku nchito yace; ndipo iye anapereka cikho m'manja a Farao.

22. Koma anampacika wophika mkate wamkuru; monga Yosefe anawamasulira.

23. Koma wopereka cikho wamkuru sanakumbukira Yosefe, koma anamuiwala.

Werengani mutu wathunthu Genesis 40