Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 4:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Kaini ndipo ananena ndi Abele mphwace. Ndipo panali pamene anali kumunda, Kaini anamuukira Abele mphwace, namupha,

9. Yehova ndipo anati kwa Kaini, Ali kuti Abele mphwako? Ndipo anati, Sindidziwai: kodi ndine woyang'anira mphwanga?

10. Ndipo anati, Wacita ciani? Mau a mwazi wa mphwako andipfuulira Ine kunthaka.

11. Tsopano ndiwe wotembereredwa kunthaka, Imene inatsegula pakamwa pace kulandira pa dzanja lako mwazi wa mphwako:

12. pamene udzalima panthaka siidzaperekanso kwa iwe mphamvu yace: udzakhala wothawathawa ndi woyendayenda pa dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Genesis 4