Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 4:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. koma sanayang'anira Kaini ndi nsembe yace. Kaini ndipo anakwiya kwambiri, niigwa nkhope yace.

6. Ndipo Yehova anati kwa Kaini, Ukwiyiranji? Yagweranji nkhope yako?

7. Ukacita zabwino, sudzalandiridwa kodi? Ukaleka kucita zabwino, ucimo ubwatama pakhomo: kwa iwe kudzakhala kulakalaka kwace, ndipo iwe udzamlamulira iye.

8. Kaini ndipo ananena ndi Abele mphwace. Ndipo panali pamene anali kumunda, Kaini anamuukira Abele mphwace, namupha,

9. Yehova ndipo anati kwa Kaini, Ali kuti Abele mphwako? Ndipo anati, Sindidziwai: kodi ndine woyang'anira mphwanga?

Werengani mutu wathunthu Genesis 4