Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 39:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo mkazi anagwira iye copfunda cace, nati, Gona ndi ine; ndipo anasiya copfunda cace m'dzanja lace nathawa, naturukira kubwalo.

13. Ndipo panali pamene mkazi anaona kuti anasiya copfunda cace m'dzanja lace, nathawira kubwalo,

14. anaitana amuna a m'nyumba yace, nanena ndi iwo kuti, Taonani, walowetsa kwa ife Mhebri kuti atiseke ife, analowa kwa ine kugona ndi ine, ndipo ndinapfuula ndi mau akuru:

15. ndipo panali pamene iye anamva kuti ndinakweza mau anga ndi kupfuula, iye anasiya copfunda cace kwa me nathawira kubwalo.

16. Ndipo anasunga copfunda cace cikhale ndi iye kufikira atabwera kwao mbuyace.

Werengani mutu wathunthu Genesis 39