Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 37:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yakobo anakhala m'dziko limene anakhalamo mlendo atate wace, m'dziko la Kanani.

2. Mibadwo ya Yakobo ndi iyi: Yosefe anali wa zaka khumi ndi zisanu ndi ziwiri analinkudyetsa zoweta pamodzi ndi abale ace; ndipo anali mnyamata pamodzi ndi ana a Biliha, ndi ana amuna a Zilipa, akazi a atate wace; ndipo Yosefe anamfotokozera atate wace mbiri yao yoipa.

3. Koma Israyeli anamkonda Yosefe koposa ana ace onse, pakuti anali mwana wa ukalamba wace; ndipo anamsokera iye malaya amwinjiro.

4. Ndipo abale ace anaona kuti atate wace anamkonda iye koposa abale ace onse: ndipo anamuda iye, ndipo sanathe kulankhula ndi iye mwamtendere.

5. Yosefe ndipo analota loto, nawafotokozera abale ace; ndipo anamuda iye koposa.

6. Ndipo iye anati kwa iwo, Tamvanitu loto limene ndalota:

7. pakuti taonani, ndinalinkumanga mitolo m'munda, ndipo taonani, mtolo wanga unauka nuima ciriri! ndipo taonani, mitolo yanu inadza niuzinga kwete, niuweramira mtolo wanga.

8. Abale ace ndipo anati kwa iye, Kodi udzakhala mfumu yathu ndithu? kapena udzatilamulira ife ndithu kodi? ndipo anamuda Iye koposa cifukwa ca maloto ace ndi mau ace.

Werengani mutu wathunthu Genesis 37