Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 34:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo ana ace amuna a Yakobo anayankha Sekemu ndi Hamori atate wace monyenga, nanena, popeza anamuipitsa Dina mlongo wao,

14. nati kwa iwo, Sitingathe kucita ici, kupereka mlongo wathu kwa mwamuna wosadulidwa; cifukwa kumeneko ndiko kuticepetsa ife.

15. Koma apa pokha tidzakubvomerezani: ngati mudzakhala onga ife ndi kudulidwa amuna onse;

16. pamenepo tidzakupatsani inu ana athu akazi, ndipo tidzadzitengera ana anu akazi, ndipo tidzakhala pamodzi ndi inu, ndi kukhala mtundu umodzi.

17. Koma mukapanda kutimvera ndi kusadulidwa, pamenepo tidzatenga mwana wathu wamkazi, ndi kumuka naye.

18. Mau ao ndipo anakomera Hamori ndi Sekemu mwana wace wa Hamori.

Werengani mutu wathunthu Genesis 34