Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 33:18-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo Yakobo anafika ndi mtendere ku mudzi wa Sekemu umene uli m'dziko la Kanani, pamene anacokera ku Padanaramu; namanga tsasa pandunji pa mudzipo.

19. Ndipo anagula ndi ndalama zana limodzi dera la munda kumeneko anamanga bema wace, pa dzanja la ana ace a Hamori atate wace wa Sekemu.

20. Ndipo anamanga pamenepo guwa la nsembe, nacha pamenepo EleloheIsrayeli.

Werengani mutu wathunthu Genesis 33