Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 33:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo Yakobo anankabe ulendo wace ku Sukoti, namanga nyumba yace pamenepo, namanga makola a zoweta zace: cifukwa cace dzina lace la kumeneko ndi Sukoti.

18. Ndipo Yakobo anafika ndi mtendere ku mudzi wa Sekemu umene uli m'dziko la Kanani, pamene anacokera ku Padanaramu; namanga tsasa pandunji pa mudzipo.

19. Ndipo anagula ndi ndalama zana limodzi dera la munda kumeneko anamanga bema wace, pa dzanja la ana ace a Hamori atate wace wa Sekemu.

20. Ndipo anamanga pamenepo guwa la nsembe, nacha pamenepo EleloheIsrayeli.

Werengani mutu wathunthu Genesis 33