Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 32:25-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo pamene anaona kuti sanamlaka, anakhudza nsukunyu ya ncafu yace; ndipo nsukunyu ya ncafu yace ya Yakobo inaguluka, pakulimbana naye.

26. Ndipo iye anati Ndileke ndimuke, cifukwa kulinkuca. Ndipo Yakobo anati, Sindidzakuleka iwe kuti umuke, ukapanda kundidalitsa ine.

27. Ndipo iye anati kwa Yakobo, Dzina lako ndani? Nati iye, Yakobo.

28. Ndipo anati, Dzina lako silidzachedwanso Yakobo, koma Israyeli, cifukwa unayesana naye Mulungu ndithu, ndipo unapambana.

29. Yakobo ndipo anafunsa iye, nati, Undiuze ine dzina lako. Ndipo iye anati, Undifunsa dzina cifukwa ninji? Ndipo anamdalitsa iye pamenepo.

30. Ndipo anacha dzina la malo amenewo, Penieli: cifukwa ndaonana ndi Mulungu nkhope ndi nkhope, ndipo wapulumuka moyo wanga,

31. Ndipo kudamcera iye pamene analoloka pa Penieli, ndipo iye anatsimphina ndi ncafu yace.

32. Cifukwa cace ana a Israyeli samadya ntsempha ya thako iri pa nsukunyu ya ncafu kufikira lero: cifukwa anakhudza nsukunyu ya ncafu ya Yakobo pa ntsempha ya thako.

Werengani mutu wathunthu Genesis 32