Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 32:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. ndiponso muziti, Ndiponso, taonani, kapolo wanu Yakobo ali pambuyo pathu, Pakuti anati, Ndidzampembedzera iye ndi mphatso imene ipita patsogolo panga, pambuyo pace ndidzaona nkhope yace; kapena adzandilandira ine.

21. Momwemo naolotsa mphatso patsogolo pace: ndipo iye yekha anagona usiku womwewo pacigono.

22. Ndipo anauka usiku womwewo, natenga akazi ace awiri, ndi adzakazi ace awiri, ndi ana ace amuna khumi ndi mmodzi, naoloka pa doko la Yaboki.

23. Ndipo anawatenga iwo nawaolotsa pamtsinje, naziolotsa zonseanalinazo.

24. Ndipo anatsala Yakobo yekha; ndipo analimbana naye munthu kufikira mbandakuca.

25. Ndipo pamene anaona kuti sanamlaka, anakhudza nsukunyu ya ncafu yace; ndipo nsukunyu ya ncafu yace ya Yakobo inaguluka, pakulimbana naye.

Werengani mutu wathunthu Genesis 32