18. pomwepo uziti, Za kapolo wanu Yakobo; ndizo mphatso yotumizidwa kwa mbuyanga Esau; taonani ali pambuyo pathu.
19. Ndipo anauzanso waciwiri ndi wacitatu, ndi onse anatsata magulu, kuti, Muzinena kwa Esau cotero, pamene mukomana naye:
20. ndiponso muziti, Ndiponso, taonani, kapolo wanu Yakobo ali pambuyo pathu, Pakuti anati, Ndidzampembedzera iye ndi mphatso imene ipita patsogolo panga, pambuyo pace ndidzaona nkhope yace; kapena adzandilandira ine.
21. Momwemo naolotsa mphatso patsogolo pace: ndipo iye yekha anagona usiku womwewo pacigono.