Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 31:43-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

43. Ndipo Labani anayankha nati kwa Yakobo, Akaziwa ndiwo ana anga, anawa ndiwo ana anga, zowetazi ndizo zoweta zanga ndi zonse ulinkuziona ndizo zanga: nanga ndidzacitira ine ciani lero kwa ana anga akazi amenewa, kapena ana ao amene anabala?

44. Tsopano tiyeni tipangane pangano, ine ndi iwe; likhale mboni pakati pa ine ndi iwe.

45. Ndipo Yakobo anatenga mwala, nauimiritsa.

46. Ndipo Yakobo anati kwa abale ace, Sonkhanitsani miyala; ndipo anasonkhanitsa miyala nakundika mulu: ndipo anadya pamulupo.

47. Ndipo Labani anacha pamenepo Yegara-sahaduta; koma Yakobo anacha Galeeda.

48. Ndipo Labani anati, Muluwu ndiwo mboni pakati pa ine ndi iwe lero. Cifukwa cace anacha dzina lace, Galeeda;

Werengani mutu wathunthu Genesis 31