4. Ndipo Yakobo anatumiza naitana Rakele ndi Leya adze kubusa ku zoweta zace,
5. ndipo anati kwa iwo, Ndiona ine nkhope ya atate wanu kuti siindionekera ine monga kale; koma Mulungu wa atate wanga anali ndi ine.
6. Ndipo inu mudziwa kuti ndi mphamvu zanga zonse ndatumikira atate wanu.
7. Ndipo atate wanu wandinyenga ine, nasinthanitsa malipilo anga kakhumi; koma Mulungu sanamlole iye andicitire ine coipa.
8. Akati cotero, Zamathotho-mathotho zidzakhala malipilo ako, zoweta zonse zinabala zamathotho-mathotho; ndipo akati iye cotere, Zamipyololo-mipyololo zidzakhala malipilo ako, ziweto zonse zinabala mipyololo-mipyololo.
9. Comweco Mulungu anazicotsa zoweta za atate wanu, nandipatsa ine.
10. Ndipo panali potenga mabere ziwetozo, ine ndinatukula maso anga, ndipo ndinapenya m'kulota, taonani, atonde okwera ziweto anali amipyololo-mipyololo, amathotho-mathotho, ndi amaanga-maanga.
11. Mthenga wa Mulungu ndipo anati kwa ine m'kulotamo, Yakobo; nati ine, Ndine pano,
12. Ndipo anati, Tukulatu maso ako, nuone, atonde onse amene akwera zoweta ali amipyololo-mipyololo, amathotho-mathotho, ndi amaangamaanga: cifukwa ndaona zonse zimene Labani akucitira iwe.
13. Ine ndine Mulungu wa ku Beteli, kuja unathira mafuta pamwala paja, pamene unandilumbirira ine cilumbiriro: tsopano uka, nucoke m'dziko lino, nubwerere ku dziko la abale ako.
14. Ndipo Rakele ndi Leya anayankha, nati kwa iye, Kodi tiri nalonso gawo kapena colowa m'nyumba ya atate wathu?