Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 31:17-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo anauka Yakobo nakweza ana ace ndi akazi ace pa ngamila;

18. ndipo ananka nazo zoweta zace zonse, ndi cuma cace conse anacisonkhanitsa, zoweta zace anaziona m'Padan-aramu, kuti anke kwa Isake atate wace ku dziko la Kanani.

19. Ndipo Labani ananka kukasenga nkhosa zace: ndipo Rakele anaba aterafi a atate wace.

20. Ndipo Yakobo anathawa kwa Labani Msuriyamobisika, m'mene sanamuuzeiye kuti analinkuthawa.

21. Ndipo anathawa iye ndi zonse anali nazo: ndipo anauka naoloka panyanja naloza nkhope yace iyaog'anire ku phiri la Gileadi.

22. Tsiku lacitatu anamuuza Labani kuti Yakobo wathawa.

23. Ndipo iye anatenga abale ace pamodzi naye, namlondola iye ulendo wa masiku asanu ndi awiri: nampeza iye pa phiri la Gileadi.

24. Ndipo Mulungu anadza kwa Labani Msuriya usiku, nati kwa iye, Tadziyang'anira wekha, usanene kwa Yakobo kapena zabwino kapena zoipa,

Werengani mutu wathunthu Genesis 31