Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 31:14-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo Rakele ndi Leya anayankha, nati kwa iye, Kodi tiri nalonso gawo kapena colowa m'nyumba ya atate wathu?

15. Kodi satiyesa ife alendo? cifukwa anatigulitsa ife, nathanso kuononga ndalama zathu.

16. Cifukwa kuti cuma conse Mulungu anacicotsa kwa atate wathu ndi cathu ndi ca ana athu; tsono, zonse wakunenera iwe Mulungu, ucite.

17. Ndipo anauka Yakobo nakweza ana ace ndi akazi ace pa ngamila;

18. ndipo ananka nazo zoweta zace zonse, ndi cuma cace conse anacisonkhanitsa, zoweta zace anaziona m'Padan-aramu, kuti anke kwa Isake atate wace ku dziko la Kanani.

19. Ndipo Labani ananka kukasenga nkhosa zace: ndipo Rakele anaba aterafi a atate wace.

20. Ndipo Yakobo anathawa kwa Labani Msuriyamobisika, m'mene sanamuuzeiye kuti analinkuthawa.

21. Ndipo anathawa iye ndi zonse anali nazo: ndipo anauka naoloka panyanja naloza nkhope yace iyaog'anire ku phiri la Gileadi.

22. Tsiku lacitatu anamuuza Labani kuti Yakobo wathawa.

23. Ndipo iye anatenga abale ace pamodzi naye, namlondola iye ulendo wa masiku asanu ndi awiri: nampeza iye pa phiri la Gileadi.

24. Ndipo Mulungu anadza kwa Labani Msuriya usiku, nati kwa iye, Tadziyang'anira wekha, usanene kwa Yakobo kapena zabwino kapena zoipa,

25. Ndipo Labani anakomana naye Yakobo. Ndipo Yakobo anamanga hema wace m'phirimo: ndipo Labani ndi abale ace anamanga m'phiri la Gileadi.

26. Ndipo Labani anati kwa Yakobo, Wacitanji? Wathawa kwa ine mobisika ndi kutenga ana anga akazi, monga mikoli ya lupanga.

27. Wathawanji iwe mobisika, ndi kundicokera kutseri, osandiuza ine, kuti ndikadakumukitsa iwe ndi kusekerera ndi nyimbo ndi lingaka ndi zeze?

28. Ndipo sunandiloleza ine ndimpsompsone ana anga amuna ndi akazi? wapusa iwe pakucita cotero.

29. M'dzanja langa muli mphamvu yakucitira iwe zoipa koma Mulungu wa atate wako anati kwa ine usiku walero, kuti, Tadziyang'anira wekha, usanene kwa Yakobo kapena zabwino kapena zoipa.

Werengani mutu wathunthu Genesis 31